POEM BY FUNNY JAMES FROM MPONDAS CDSS CFT CLUB

Open your eyes kwacha tambala akalila kwacha

Eni malonda tiyeni tikapange ma kwacha

Musakonde tulo pakadafunda galu adajiwa

 

Malonda anuwo musawonjeze msuzi ayikeni

Poyera anthu aziwona okha musayike

Muthumba ngati malonda amphaka

 

Competition and Fair Trading Commission (CFTC)

Bwenzi lenileni kwa onse ochita

Malonda, iwowatu abwera ndi ulangizi ndi

Upangiri pa malonda anuwo

 


Malonda anuwo ogula ndi ogulitsa alindi

Ufulu okadandaula ku CFTC ngati

Wamenyedwa m’mimba likuswa mtengo

 

Malonda anuwo musawonjeza deya mudiwa

Wachiwona ndani bwanji muchepetse

Musachite zinthu mosokoneza dala poti

Mudzalapa atayeza mkhosi

 

Malonda anuwo musagulitse zinthu zomwe

Zidapanga expire chifukwa mudzawona

Ngati chauta wakondera atakukwidzingani

Palibe za ninvela apa pawawa

Ndipo pa malonda anuwo musabele anthu

Posemphanisa mitengo mwadala

Pangati chilungamo kuti zanu ziyende

 

Cholinga cha bungweli si kukubelani kapena kukuwopsyezani

Kapena kukubelani ayi koma chake cholinnga

Ndi chilungamo pa malonda, kuphunzita

Ndi kuziwitsa za ufulu wa ogula

Ndi ogulitsa kuti pasakhale chinyengo

 

Malonda anuwo ngati utsizina mtole udayendapo

Ndithu chanu chibalo cha sayizi yanu

Kuti mukaphunzire chilungamo pa malonda

 

Ndipo muzalipila lupiya lokwana K500, 000

Kapena kukagwira ntchito yakalavula gaga

Kwa dzilimika dzisano musadzati sindidanene

Za mpikisano oyenera pa malonda

 

Chofunika nkupanga chinvano cha mawu ngati amayi anvano

Ndi bungwe la Competition and Fair Trading Commission (CFTC)

Mudzamanga mansion ku mission

 

Ikakhala ntchezi idanva ndi liwu limodzi

Chikakhala chibweleza chidathetsa nkhunda

Kukhala nguluwe idakumbuka amake nsampha

Utaning’a