MPIKISANO WOYENERA PA MALONDA

Poem by Leornard Phiri from Mpondas CDSS CFT Club

 

Mpikisano woyenera pa malonda

Ndi m’nasi wakutsina phirikanilo

Wakuolotsa mbuna wakukonda

Tisawonjere deya mudiwa

Khani yalunjika pa malonda anuwo

 

Kaya ndinu ogulitsa ma sweet,

zimbwyende ndi mandasi

Musayese zida poti gulitsa malonda anu

Omwe anapanga expire

 

 

Mpikisano oyenera pa malonda

Tigulitseni zinthu zoyenera pa malonda

Mu nthawi yake

 

Chiyipira wachaje amake amati ndi mwana

Malonda anuwo musawaonele mubotolo

Mandasi, zigumu ndi ukadya ubwelele

Zomwezi lina tsiku mukafusa mtengo

Wa tayala la sienta

Mpikisano oyenera pa malonda

Tigulitseni malonda achilungamo

Osakhala za usizina mtole

Muwulawa unyolo

Ndipo mukapezeka mukugulitsa

Zinthu expire komanso zakuba

Mukwizingidwa komanso

Mufupa chosavina polipira

Chindapusa cha K500,000

 

Mpikisano oyenera pa malonda

Ogulitsa malonda inu

Mupewe nchitidwe oipa ngati

Kukhazikitsa mtengo umodzi pakati

Panu, Kubitsa kapena kuononga

Katundu ndi cholinga chofuna

Kukweza mtengo ndi kugulitsa zinthu

Zoopsya pa moyo, mukatelo

Malonda anu azakupindulilani

 

Mpikisano oyenera pa malonda

Tsono tadyani mutu pa samu

Imeneyi bola wanu mwana

Asalilire kuti adadi mukundimana

K30, 000 koma akuti ulipile

K500, 000 mayi Kalanga ine

Kupambana kuchiza kulewa

Ndipange dala anapita ndi madzi

Mpikisano oyenera pa malonda